14/04/2026
TITHANDIZENI NDI
ZOCHEPA ZOMWE MULI NAZO,
ULENDO WOKACHEZA NDI AMAYI OYEMBEKEZERA:
Okondedwa anzanthu inu, amtima wabwino ndi ofunira zabwino
Ife a Bungwe la Mphatso the Gift Foundation , timakhulupirira kuti Mwana aliyense ndi m'dalitso, ndipo Mayi aliyense akuyenera kuthandizidwa ndi kulemekezedwa—makamaka pa nthawi ya msautso.
Monga bungwe lachifundo lachikhristu lokhazikika pa chikhulupiliro, lodzipereka kuthandiza ana amasiye, ana osauka, komanso okalamba, timadziwa kuti kuthyola unyolo wa umphawi kumayambira pomwe moyo umayamba.
Pa 4 July 2026, ku Machinjiri mu mzinda wa Blantyre,
Bungwe lathu la Mphatso the Gift Foundation tikupita pa chipatala cha
South Lunzu
(ku Maternity Ward),
Kukacheza ndi kukapereka 'Mphatso ya Chiyembekezo' kwa amayi a oyembekezera ndi omwe angobeleka kumene.
Tsiku li tizapeleka mphatso zosiyanana monga:
Zitenje, Mabeseni, mabigiliri, Sopo wosambira komanso wochapila, Sugar, matches, makandulo, ndi zina zofunikira.
Mphatso zi tikuzapeleka ngati njira imodzi ya uthenga wachikondi, wosonyeza amayi olimba mtima awa kuti sali okha ayi, sanaiwalike,
Tikupita m'chipinda cha amayi obereka (maternity ward)
kuti tikapereke chitonthozo kwa omwe akukumana ndi kufika kwa moyo watsopano ndi kusadziwa kapena mantha
Ife a Bungwe la Mphatso the Gift Foundation
Tikupempha chithandizo kwa inu nonse akufuna kwabwino ndi omvetsetsa ntchito za chifundo kuti mutithandize potigulira zinthu zomwe zatchulidwazi,
M***a kutithandiza ndi ndalama iliyonse yomwe mungathe Kuti ntchito ikwanilitsidwe komanso izayende bwino
Lowani nawo m'gulu lathu paulendo wokayankhula mawu olimbikitsa ndikufalitsa uthenga wabwino wa chikondi pa chipatala chi
(1 Akorinto 13:1-13)
KUTI MUTHANDIZE:
9100004034578
(Mphatso Limbanga)
Blantyre Branch
+265893232710
(Mphatso Limbanga)
+265995690336
(Mphatso Limbanga)
kuti mumve zambiri zokhuza ntchito ya chifundo yi imbani phone pa
+265 888 878 678
Blantyre, Malawi